African Storybook
Menu
Ganizani ndi Poto Wakufa
Bether Mwale-Moyo and Moffat Moyo
Emily Berg
CiNyanja
Kalekale, panali munthu wina dzina lake Ganizani, amene anali ndi ng'ombe imodzi. Tsiku lililonse, Ganizani amadyetsa ng'ombe yake.

Iye amaipatsanso madzi akumwa, koma iye anali cabe ndi kapoto kakang'ono kamadzi.
Conco, iye anapita kunyumba kwa aneba ake kuti abwerekeko poto waukulu wa madzi.

Aneba ake anvomera kumubwereka mbiya ya madzi, nati, "Vuto la neba wanga ndi vuto langanso."
Patapita masiku ocepa, Ganizani anapita kwa woumba mbiya, nagula kapoto kakang'ono. Anapita nako kunyumba.

Anakakaika m'kati mwa poto waukulu umene anabwereka uja kwa aneba ake.
Pambuyo pake, iye anaika poto waung'ono m'kati mwa poto waukulu, nausenza pamutu pake.

Anabweza poto wakulu uja anabwereka kwa mnzake.
Ganizani anamuuza mnzake kuti, "Ndabweretsa poto uja ndinabwereka, wabereka poto unzake."

Neba wake uja anadabwa kwambiri kuti poto wake wabereka poto wina. Anamuyamikira Ganizani kuti, "Banja lako ndi lodalitsika."
Patapita masiku ocepa, Ganizani anapitanso kwa neba wake uja ndi kubwerekanso poto waukulu uja.

Iye analibe zolinga zabwino.
Mwini wapoto waukulu anayembekezera mosangalala kuti Ganizani abweze poto wake.

Potsirizira pake, iye analondola Ganizani kunyumba kwake nati, "Ndabwera kudzatenga poto wanga."
Ganizani anauza neba wake kuti, "Mnzanga, poto wako uja unafa. Pano, ndinali kukonzekera kubwera kwanu kuti ndikuuze za nkhani yacisoni imeneyi."
Mnzake uja anawomba m'manja modabwa. Nkhope yake inasintha ndi mkwiyo.

Anamukalipira Ganizani, "Sindinamvepo za poto kufa!"
Ganizani anayankha nati, "Mnzanga, uyenera kuvomera zinthu izi. Cinthu ciliconse cimene cimabereka ciyenera kufa. Nanenso ndinali ndi cisoni ndi imfa ya poto waukulu."
Mnzake anakwiya kwambiri ndipo anapita kubwalo lamilandu kumphala. Amfumu anamvetsera ku madandaulo a awirirwo.

Iwo anapeza kuti mwini wa poto anali wolakwa ndipo anaweruza kuti Ganizani akasunge poto wakufawo.
"Pamene Ganizani anakuuza kuti poto inabereka, unavomera. Pamene iye akuti ciliconse cimene cimabereka ciyenera kufa, iye ananena zoona."

Umu ndi mmene woweruza anaweruzira mlandu.
Mnzake wa Ganizani anapita kunyumba ngati nkhono.

Ganizani anatenga poto kamba kakuchenjela kwake.
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
Ganizani ndi Poto Wakufa
Author - Peter Kisakye
Adaptation - Bether Mwale-Moyo and Moffat Moyo
Illustration - Emily Berg
Language - CiNyanja
Level - Longer paragraphs
© Text: Uganda Community Libraries Association (Ugcla) Artwork: African Storybook Initiative 2015
Creative Commons: Attribution 4.0
Source www.africanstorybook.org
Original source http://ugcla.org
Menu
  • Navigate

    Navigate through the story by swiping right or left or clicking when the cursors changes to an arrow on the right or the left edge of the screen.

    Tap or click on the centre of the page to see, or remove the menu bars at the top and the bottom of the screen. You can also use the ESC key.

    You can use the slider at the bottom as a way to move quickly through the story. On a mobile device tap on the slider before you drag the slider button.

    Click or tap to return to African Storybook.

  • Share
    If you have a Twitter or Facebook account, you can share this story on your page or a page you manage. You can also copy the web link (URL) for this story.
    • Twitter
    • Facebook
    • Url
  • Rate
    Other visitors rated this story

    Tell us how much you liked the story – drag the scroller to highlight one or more stars
    • Submit
  • Comment
    Read other people’s comments on the story, or add your own.
    • Enter your comment
    • Name
    • E-mail
    • Post
  • Translations and adaptations
    • Byantaka anongo ifwiide
      ChiTonga (Translation)
    • Byantaka anongo ifwiide
      ChiTonga (Adaptation)
    • Byantaka na Poto Yakufa
      CiNyanja (Translation)
    • Byantaka and the dead pot
      English (Translation)
    • The pot that died
      English (Adaptation)
    • Dambu Kashe Mai Zari
      Hausa (Nigeria) (Translation)
    • Byantaka noomutondo waafwa
      IciBemba (Translation)
    • Malumo na umutondo waafwa
      IciBemba (Adaptation)
    • Ntampaka n'intango yapfuye
      Kinyarwanda (Translation)
    • Chungu kilichokufa
      Kiswahili (Translation)
    • Biantaka na chungu kilichokufa
      Kiswahili (Translation)
    • Byantaka ne Entamu Eyafa
      Lusoga (Original)
    • Ensugha eyafa
      Lusoga (Translation)
    • Agulu Na Atoani
      Ng’aturkana (Translation)
    • Inyungu yafwa
      Oluwanga (Translation)
    • Ensoha Eyafire
      Runyoro (Translation)
    • እታ ዝሞተት ዕትሮ
      Tigrigna (Translation)
  • Download to read
    Landscape version
  • Download to print
    Portrait (booklet) version
  • Download EPUB