Aphunzitsi a Akinyi
Lawrence A. Konjuro
Vusi Malindi

Awa ndi aphunzitsi anga. Ndipo dzina lawo ndi a Akinyi.

Iwo amatikonda kwambiri.

1

Aphunzitsi awa amatiphunzitsa kuwerenga.

Amatiphunzitsa zilembo za mavawelo. Ndingawerenge zilembo a. e, i, o, u.

2

Aphunzitsi Akinyi amatiphunzitsa za utoto monga kufiira, kubiriwira, msipu, cikasu ndi kuda.

3

Pa nthawi yogona, Aphunzitsi Akinyi amatiimbira nyimbo yogonera.

4

Nyimbo yogonera imaimbidwa tere:

Lulu wee, Lulu wee,
Mwana akalira ndi njala,
Mwana akalira ndi tulo,
Mwana akalira ndi njala,
Mwana akalira ndi tulo.

5

Aphunzitsi Akinyi amadziwa kunena nthano zambiri.

Tsiku lililonse la mlungu, iwo amatiuza nthano zosiyanasiyana.

6

Patsiku Lolemba, amatiuza nthano za amuna amene anacita zinthu zazikulu.

7

Patsiku Laciwiri, amatiuza nthano za azimayi amene anacita zinthu zaikulu.

8

Patsiku Lacitatu, amatiuza nthano zonena za mayendedwe.

9

Patsiku Lacinayi, amatiuza nthano zaulimi.

10

Ndipo patsiku Lacisanu, timakamba nthano zathu patokha.

11

Aphunzitsi athu ndi abwino koposa m'dziko lonse.

Ndikakula, ndifuna kuti ndikakhale ngati Aphunzitsi a Akinyi.

12
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
Aphunzitsi a Akinyi
Author - Lawrence A. Konjuro
Adaptation - Bether Mwale-Moyo, Moffat Moyo
Illustration - Vusi Malindi
Language - CiNyanja
Level - First sentences