Selemeng amakonda acona.
Pali acona ambiri pakhomo pawo.
Selemeng ali ndi cona m'modzi wakuda.
Cona ameneyu amadya kwambiri.
Selemeng ali ndi cona m'modzi wonenepa.
Cona ameneyu amadya cinthu ciliconse.
Cona wacitatu, wakwera mu mtengo.
Cona uyu waphata mu mtengo.
Selemeng wakwera mu mtengo. Nayenso waphata pamodzi ndi cona wacitatu.
Amake Selemeng afunika kuwathandiza kutsika mu mtengo.
Selemeng ali ndi acona awiri aulesi.
Iwo amakonda kugona padzuwa tsiku lonse.
Selemeng ali ndi acona atatu otakataka.
Iwo amagwira makoswe usiku wonse m'khichini.
Selemeng ali ndi galu m'modzi. Dzina la galu uyu ndi Lirafi.
Lirafi alibe anzake. Iye ndi wosakondwa.
Acona samakonda Lirafi.
Amamuthamangitsira panja panyumba.
Lirafi amathawa.
Selemeng wapeza Lirafi ndipo akumubwerertsa kunyumba. Acona sanakondwere.
Safuna kuonanso Lirafi
Kodi Selemeng ali ndi acona angati?
Iye ali ndi acona asanu ndi atatu.
Kodi Selemeng ali ndi agalu angati? Iye ali ndi galu m'modzi cabe.
Kodi Lirafi alikuti tsopano?
Kodi muli na acona angati pakomo panu?
Muli ndi galu zingati pakomo panu?