Njinga ya nyimbo ya Takondwa
Diana Tebeila
Diana Tebeila

Takondwa amakonda kusangalala.

Takondwa amayendera njinga.

Abale ake ndi anzake amamukonda kwambiri.

1

Takondwa amakonda nyimbo.

Anzake amakonda kuvina ndi kumuikira nyimbo.

2

Anzake a Takondwa anaika sipika yomverera nyimbo pa njingayo .

Akadina batani mbali inayi, nyimbo zimalira.

3

Takondwa amatha kudziongola ndi kuvina panjinga yake.

Amayesera kuvina payekha, kenako amavina ndi anzake.

4

Tsiku lina anzake anaona mpikisano ovina utalengezedwa munyuzipepala.

Anawafusa mayi a Takondwa ngati angakalembetse ku mpikisanowo.

Mayi a Takondwa anavomera.

5

Anzake a Takondwa anabwereka foni ya mayi ake ndi kujambula mavinidwe awo.

Anamujambula Takondwa akuvina nyimbo ya kumtima kwake, kenako anatumiza mavinidwewo kumpikisano.

Takondwa anamusankha kukachita nawo mpikisano!

6

Tsiku la mpikisano linafika.

Takondwa anavala malaya ake a nyuwani.

Nyimbo zitayamba, anayenda mwadongosolo ndi mokondwa.

7

Anthu ochemerera anakuwa, "Takondwa! Takondwa!"

Zoona zake, anali dolo ovina tsiku limenelo.

Takondwa anapambana ndipo analandira mphoto zambiri.

8
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
Njinga ya nyimbo ya Takondwa
Author - Diana Tebeila
Translation - Peter Msaka
Illustration - Diana Tebeila
Language - ChiChewa
Level - Longer paragraphs