Sukulu yathu yapamwamba
Juwayiliya Bunaya
Yankho Jere

M'mudzi wina waung'ono kuMalawi, munali sukulu yapamwamba.

Inkatchdewa kuti Chiko, chidule cha dzina loti chikondi.

1

Sukulu yathu inali malo opereka chiyembekezo ndi chikondi.

Inali sukulu ya ana amasiye monga ine.

2

Sukulu yathu inazunguliridwa ndi maluwa amitundu yokongola yosiyanasiyana.

Panali ofiira mowala kwambiri, achikasu, ndi amtambo.

Sukulu yathu anali malo osangalalirako.

3

Ogwira ntchito pa sukuluyi ankatipatsa chakudya ndi mayunifolomu.

Izi zinatichititsa kumva kuti ndife otetezeka komanso okondedwa.

4

Chipanda sukulu imeneyi, sindikanadziwa kuwerenga ndi kulemba.

Sindikanaphunzira kuwerengetsera manambala kapena kudziwa nkhani zosangalatsa m'mabuku

5

Aphunzitsi ndi ogwira ntchito pa sukuluyi anali ngati abale athu.

Ankatichititsa kumva kuti ndife ofunikira komanso okondedwa.

6

Tsiku lililonse ku sukulu tinkaphunzira zinthu zatsopano.

Tinaphunzira ubwino wothandiza ena ndi kukhala othokoza pa zomwe tinali nazo.

7

Sukulu yanga siinandiphunzitse kuwerenga ndi kulemba kokha komanso inandiphunzitsa kukhala munthu wabwino.

Inandionetsa kuti ndi chikondi, chisoni, ndi maphunziro, titha kuthana ndi chilichonse.

8
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
Sukulu yathu yapamwamba
Author - Juwayiliya Bunaya, Zahira Suwedi
Translation - Peter Msaka
Illustration - Yankho Jere
Language - ChiChewa
Level - First paragraphs