Mtsikana wachilungamo
Ann Logialan
Jacob Kono

Kunali mtsikana wina wokongola.

Tsiku lina, anali ndi njala kwambiri. Anaganiza za njira yopezera chakuti adye.

1

Anakumana ndi bambo yemwe anamufunsa, "Ulibwanji mtsikana? Chakukwiyitsa ndi chiyani?"

Mtsikanayu anayankha, "Ndili ndi njala."

2

Bamboyo anamumvera chisoni mtsikanayu. Anamuuza kuti munali phwando m'mudzimo ndipo apite kumeneko akabe chakudya.

Mtsikanayu anali asanabepo ndi kale lonse.

3

Iye anadzuka mwachangu ndi kupita ku nyumba komwe kumachitikira phwandolo.

4

Atayandikira, anayiwala malangizo obera aja. Anayimba mobwerezabwereza:
Ndabwera kudzaba chakudya, cha-ku-dya,
ndikuyenda pang'onopang'ono, pang'onopang'ono.

5

Anthu anayamba kumva nyimbo ya mtsikanayo ali patali mpaka anafika pa malo aphwandowo.

6

Anthu anali odabwa ndi mtundu wa nyimboyo ndipo anamufunsa, "Ukuchokera kuti? Ukufuna chiyani? N'chifukwa chani ukuyimba?"

7

Mtsikanayu anawauza kuti anali ndi njala ndipo anamupatsa chakudya.

Kenako, analangizidwa kuti kuba ndi koyipa.

8
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
Mtsikana wachilungamo
Author - Ann Logialan
Translation - Peter Msaka
Illustration - Jacob Kono
Language - ChiChewa
Level - First paragraphs