Mwana wobweretsa mtendere
John Nga'sike
Jacob Kono

Mayi ndi mwana wake anapita kunkhalango.

Anapita kukathyola zipatso.

1

M'nkhalangomo, anapeza mtengo wa zipatso zakupsa.

2

Anagoneka pansi mwana wake amene anali mtulo, ndikukwera mumtengo.

3

Mlendo ochokera ku mudzi wina anadutsira pamene panali mwanayo. Ataona mwanayo, anali wodabwa.

Anadzifunsa yekha, "Mayi wake alikuti?"

4

Anawerama.

Phokoso la matcheni a m'khosi mwake linamudzutsa mwanayo.

5

Anamulola mwanayo kuti aseweretse matcheni akewo.

Mwanayo anasekelera posewerapo.

6

Mayi uja anayang'ana pansi kuti awone chimene mwanayo amasekerera.

Anaona munthu wachilendo.

7

Anali ndi mantha kotero anagwetsa chikwama chake cha zipatso.

8

Mlendoyo anayang'ana m'mwamba.

Ndipo anati, "Musaope, ndikungosewera ndi mwana wanu wokongolayu."

9

Kenako, mayiyo anatsika mumtengo muja.

10

Mlendoyo anatenga limodzi mwa matcheni akewo.

Anampatsa mwana uja, "Iyi ndi mphatso yako," anatero.

11

"Pitani kunyumba ndi mwana wanu. Mukawauze amuna anu akasamukire kumudzi wa mtendere. Mwana wanu wandipatsa mtendere," anatero mlendoyo.

12
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
Mwana wobweretsa mtendere
Author - John Nga'sike
Translation - Peter Msaka
Illustration - Jacob Kono
Language - ChiChewa
Level - First sentences