Cilango
Adelheid Marie Bwire
Melany Pietersen

Tsiku lina, amayi anagula zipatso zosiyanasiyana.

1

"Kodi ndi liti pomwe tingadye zipatso?" tinawafunsa.

"Tidzadya zipatso usiku uno," anayankha amayi.

2

M'bale wanga Musonda ndi womana.

Analawa zipatso zonse. Iye anadya zambiri.

3

"Onani zimene Musonda wacita," anatero m'bale wanga wamng'ono.

"Musonda ndi wosamvera ndipo ndi wodzikonda," ndinatero ine.

4

Amayi anakwiya ndi zimene anacita Musonda.

5

Ife tonse tinakwiya ndi zimene Musonda anacita.

Koma Musonda sanamve cisoni.

6

"Kodi mudzamulanga Musonda?" anafunsa m'bale wanga wamng'ono.

7

"Musonda, udzamva cisoni posacedwapa,'' anacenjeza amayi.

8

Musonda anayamba kusamva bwino.

9

"M'mimba mwanga muwawa,'' anatero Musonda motsitsa mawu.

10

Amayi anadziwa cifukwa cake Musonda anali wodwala.

"Zipatso zikumulanga Musonda,'' anaganiza tero amayi.

11

Pambuyo pake, Musonda anapepesa kwa ife. "Sindidzakhalanso waumbombo," analonjeza.

Ife tinamukhulupirira.

12
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
Cilango
Author - Adelheid Marie Bwire
Translation - Clarence K Phiri
Illustration - Melany Pietersen
Language - CiNyanja
Level - First sentences