Nsabwe yothudzulidwa
Zimbili Dlamini
Magriet Brink

Kalekale, panali anyamata awiri amene ng'ombe zawo zinasowa.

Anazinyang'ana ng'ombezo mpaka kunawadera.

1

Pamene mdima umagwa, anaona kuwala mnyumba ina.

Anagwirizana zokapempha malo ogona.

2

Anapita ku nyumba ija ndi kugogoda. Chitseko chinatsekulidwa ndipo analowa.

Anyamata aja sanaone wina aliyense. Koma anamva mawu akuwapatsa moni.

3

Mawuwo anati, "Ndine nsabwe. Vundukulani poto mutengemo chakudya. Vundukulani m'phikawo ndipo mumwe thobwa lili m'menemo."

4

Kenako nsabwe inavala chikopa chake ndikupita panja.

5

Anyamata aja anadya, anamwa ndi kuthokoza.

Kenako anatuluka m'nyumba muja.

6

Atanyamuka, anayamba kuganiza zoipa. Anati, "Ayi, sitimayenera kudya chakudya cha mnyumba ya nsabwe."

Ndipo anaganiza zobwereranso kunyumba kuja ndi kukaithudzula nsabwe ija.

7

Anabwereradi kunyumba kuja ndi kukaithudzula nsabwe.

Mwadzidzi nsabwe ija inasowa, ndipo nyumba ijanso inasowapo!

Anazindikira ali panja popanda nyumba.

8
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
Nsabwe yothudzulidwa
Author - Zimbili Dlamini
Translation - Peter Msaka
Illustration - Magriet Brink
Language - ChiChewa
Level - First paragraphs