Dzuwa lotanganika kwambiri
Mimi Werna
Joe Werna

Dzuwa limatuluka m'mawa, kuchokera ku m'mawa.

Ndimamva tambala akulira mbandakucha.

1

Dzuwa limadutsa pamwamba pa nyumba ya Tefa, chakudya cham'mawa tisanadye.

Ndimamva kununkhira kwa tiyi ndi zitumbuwa kutsatira kuwala kwadzuwa pa windo langa.

2

Dzuwa limapita kuseli kwa mitengo masana kusukulu.

Kenako limafika pa madzi odikha pakati pa bwalo losewererapo.

3

Dzuwa limayima pamwamba pa mutu wanga. Chithunzithunzi changa chimakhala pambali panga.

Timasewera masewero a chithunzithunzi ndi anzanga.

4

Chithunzithunzi changa chimakula, kenako kuchepa. Timachithamangitsa.

Chithunzithunzi changa chimatalika, kenako kufupika. Timachithamangitsa.

5

Ndimaima, anzanganso amaima. Timaona zithunzithunzi zathu zikuvina.

Timatopa kenako ndikubwereranso mkalasi. Tikaweruka timapita kunyumba.

6

Dzuwa limayasamula.

Ndimaliona dzuwa likuzimirira kumadzulo. Ndimaona chithunzithunzi changa pa khoma.

Ndi nthawi yokagona.

7

Dzuwa limatsika kuseli kwa mitambo.

Ndimagona pabedi panga, ndipo ndimalota dzuwa likupita kutali kwambiri.

8
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
Dzuwa lotanganika kwambiri
Author - Mimi Werna
Translation - Peter Msaka
Illustration - Joe Werna
Language - ChiChewa
Level - First sentences