Ngalawa ya Sara
Little Zebra Books
Rachel Greer

Sara ali na ngalawa imodzi.

Ngalawa yake ni yaikulu.

Ngalawa ili mumpepete mwa musinje.

1

Azimai ali pamusinje. Mai umozi ali ndi beseni. Mubeseni muli zipaso. Mai wina watenga mbuzi imozi. Mai winanso watenga mbuzi ziwili.

Iwo afunsa Sara: "Tingafike bwanji sidya ilo?"

Sara anena: "Lowani mungalawa yanga!"

2

Posatila, afika azibambo. Bambo umozi watenga nsomba. Wina ali ndi njinga. Winanso watenga katumba momwe muli mteza.

3

Bambo wina watenga tumatumba tuwili momwe muli mteza.

Iwo afunsa Sara: "Tingafike bwanji sidya ilo?"

Sara anena: "Lowani mungalawa yanga!"

4

Nyama zina, zafika ku msinje.

Izo zifunsa Sara: "Tingafike bwanji sidya ilo?"

Sara anena: "Lowani mungalawa yanga!"

5

Nyama zilowa mungalawa.
Galu alowa mungalawa.
Cona alowa mungalawa.
Nyani alowa mungalawa.
Kalulu alowa mungalawa.
Kamba alowa mungalawa.
Gwape alowa mungalawa.

6

Njobvu ifika pamusinje. Iyo ifunsa: "Ningacite bwanji kuti nifike sidya ilo?"

Sara anena: "Lowani mungalawa yanga!"

Njobvu ilowa mungalawa. Manzi azula mungalawa.

7

8

Ngalawa niyingono kwambili. Malo niyocepa.

9

Sara anena: "Iiiiiii! Yembekezani ntawi pangono. Coyamba nizanyamula azimai."

10

"Kaciwili, nizatenga azibambo."

11

"Pomaliza nizatenga nyama."

12

Njovu inena: "Iiiiiii! Ine niwoloka pansi!"

13
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
Ngalawa ya Sara
Author - Little Zebra Books
Translation - Manuel Gripa Kandodo
Illustration - Rachel Greer
Language - CiNyanja
Level - Longer paragraphs