Palesa akonda mitengo na maluwa
Ursula Nafula
Jesse Pietersen

Uyu ni Palesa.

Zina lake itantauza "maluwa" mucitundu ca kwao ciSetswana.

1

Kuseni Palesa anauza mutengo wa ma lalanje nati. "Iwe mutengo utipase ma lalanje yambili."

2

Palesa ayenda kusukulu.

Munjila anati kwa uzu, "Iwe uzu ukule kwambili, ndipo usafe."

3

Palesa anona maluwa yali imilile. "Imwe maluwa, zikoma pa maonekedwe anu okongola."

4

Pa sukulu, Palesa anauza kamutengo nati. "Iwe kamutengo, umela matepo akulu-akulu kuti tiziwelengela mucinfwile cako."

5

Palesa anauza mupanda wamene unazungulila sukulu lake nati, "Kula nampamvu kucinjiliza antu oyipa kungena."

6

Pamene Palesa anabwelela ku nyumba, anayenda kuona mutenga wama lalanje, "Kodi ma lalanje ako apya?"

7

"Mhm! Malalanje akali abisi," anati Palesa.  "Tizaonana mailo iwe mutengo wamalalanje," anakamba. "Kapena mailo uzankala na malalanje akupya!"

8
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
Palesa akonda mitengo na maluwa
Author - Ursula Nafula
Translation - Bether Mwale Moyo
Illustration - Jesse Pietersen
Language - CiNyanja
Level - First sentences