Mfumu ya M\\'mawa Okha
Nazinomwe Reading Group

M'mawa, tambala amagwedeza mutu wake.
Kenako amakutumula mapiko ake.

1

Tambala amalira, kokoliko! Kokolikooo!
Phokoso limamveka mudzi onse.

2

Misoti ndi anapiye zonse zimadzuka.
Anthu nawonso amadzidzimuka mtulo.

3

Anthu nawonso amadzuka.
Abambo anyamula makasu.
Amayi ayamba kuphika chakudya cha mmawa.

4

Ana asukulu ayamba kukonzekera kupita kusukulu.
Mudzi onse uyamba ntchito za tsikulo.

5

Tambala alirlanso kachiwiri.
Kudzutsa alesi onse okonda tulo.

6

Tambala ndi mfumu ya mudzi onse.
Imadzutsa aliyense.

7

Tsoka ilo, akalira masana palibe amalabada.
Ndi mfumu ya mmawa okha.

8
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
Mfumu ya M\\'mawa Okha
Author - Nazinomwe Reading Group
Illustration -
Language - ChiChewa
Level - First paragraphs