

Ndine Chikondi. Ndimakhala kufupi ndi nyanja ya Malawi.
Nyanjayi ndi yaikulu komanso yokongola kwambiri.
Kalekale anzanga akamapita kusukulu, ine ndinkathamangira kunyanja.
Ndimathamangira kunyanja koona asodzi akuwedza nsomba uku ndikulingalira zokasewera mpira masana ake.
Mayi anga sankasangalala ndi mchitidwewu.
"Chikondi, tabwera! Uchedwa kusukulu." Iwo anakalipa tsiku lina. Ndipo ndinayankha, "Ndikubwera ndatsala pang'ono."
Koma sindinapite, ndinali ndikulingalira zogoletsa zigoli kumpira masana ake.
Tsiku lina kunyanja kuja kunabwera woimba wotchuka.
Ana onse anamuthamangira chifukwa amapereka mphatso kwa ana omwe amuonetsa ntchito yomwe achita kusukulu.
"Ndionetseni kaye zomwe mwapanga kusukulu ndipo ndikupatsani mipira." Anatero woyimbayo uku akusekerera.
Ndinalibe ntchito yakusukulu yoti ndingamuonetse choncho sindinapeze nawo mpira.
Anzanga anapeza mipira yosewerera masewera a mpira wa miyendo koma ine sindinapeze kanthu.
Ndinakhala mphepete mwa nyanja uku nditakhumudwa.
Ndinakumbukira zomwe amama amanena mobwerezabwereza. "Kusamvera kumamanitsa zabwino"
Tsopano ndimapita kusukulu nthawi zonse ndisanapite kunyanja koona nsomba kapena kosewera mpira.
Ndimakaonabe nsomba zikudumpha, koma ndimayamba ndagwira ntchito yakusukulu kaye.
Kumvera amama ndi kwabwino. Nthawi zina umatha kupeza nazo mpira.

