M'dani wa Nkhuku
Impact Network Mathias Mwale

Panali nkhuku ndi mphemvu. Izi zacilengedwe zinapalana cibwenzi ndipo zinali kuyendelana kawiri - kawiri.

1

Tsiku lina nkhuku inayendera mphemvu kunyumba kwace. Mphemvu anakodwera kwambiri ndipo anakonzera nkhuku cakudya kuti idye. Nkhuku inakodwera kwambiri ndi kudya cakudya cija, itatha kudya cakudya inayamba kuceza.

2

Patapita Sabata imodzi mphemvu anaganiza kuti akayendere mzace nkhuku. Mphemvu inanyamuka ulendo opita kwa a nkhuku. Mphemvu itafika kwa a nkhuku, a nkhuku anakodwera kwambiri nalonjerana. Mosataya nthawi a nkhuku anakonza cakudya.

3

Atatha kudya a nkhuku ndi anzawo anayamba kuceza mnyumba, ndipo atatha kuceza Mphemvu anatsazika kuti apite kunyumba kwao. Nkhuku anakonza zinthu zakuti bwenzi lace linyamule monga izi: ufa, nshawa ndi zina zotero.

4

Awiriwa ananyamuka ulendo operekezana, ndipo mjira iwowa anali kukambilana nkhani zosiyana - siyana. Iwowa anayenda mtunda wautali cifukwa nkhuku inafuna kuthandiza mphemvu kunyamula zimene inapatsa mzace mphemvu.

5

Nkhuku ndi mphemvu zitayenda mtunda wautali, nkhuku inanva njala. Iyo ina ona - ona koma osaona cakudya cakuti ingadye. Motero inafuna kudya mphemvu.

6

Mphemvu atowona kuti nkhuku wamusinthira maganizo, iye anayamba kuthawa. Mphemvu tsopano inayamba kuuluka. Nkhuku nayo inayamba kuuluka. Koma cifukwa cakuti mphemvu ndi yaing'ono inauluka mofulumila kuthawa.

7

Mphemvu itawona kuti nkhuku ikubwelabe , iyo inauluka m'mwamba kwambiri. Ndipo mphemvu inathawira mnyumba ya munthu, m'mene inabisala, Nkhuku anayesetsa kufuna koma sanaionenso ai.

8

Kucokera apo mphemvu zinakhala cakudya ca nkhuku. Kotero kuti ngati nkhuku yaona mphemvu imadya kukhala ngati cakudya. kufikirana lero mphemvu zimakhala m'manyumba kubisala nkhuku kuti zingadyedwe.

9
You are free to download, copy, translate or adapt this story and use the illustrations as long as you attribute in the following way:
M'dani wa Nkhuku
Author - Impact Network Mathias Mwale
Illustration -
Language - CiNyanja
Level - First paragraphs